Owina Lotto agula nyumba ndi galimoto –

By Gracious Zinazi

Mdala Mkwinda wa zaka 57 yemwe anapata 45 million kwacha chifukwa analosera molondola ma nambala folo mu Premier Lotto wagwiritsa ntchito zina mwa ndalamazi pogula nyumba ndi galimoto.

Iwo agula nyumba yapamwamba ya 30 million kwacha ku Kanjedza mu mzinda wa Blantyre ndi galimoto yandalama zokwana 5 million kwacha.

Mzibamboyu yemwe ndi oyendetsa galimoto ku Blantyre City Council  anakhala munthu oyamba m’Malawi muno kupambana mphoto yaikulu chotero kuchoka ku Premier Lotto.

Koma ngakhale anawina, mkuluyu yemwe ndi okwatira komanso ali ndi ana anayi walangiza anthu kuti akhale olimbikira ntchito osati azigodalira mayere kapena kuti kubeta.

“Ndinapambana ndalama zankhaninkhani ngakhale sindichita mayere a Premier Bet pafupipafupi, ndimachita izi nthawi yanga yopuma pamene ndamaliza zomwe zimandipindulira m’moyo uno. Tiyeni tizi beta koma mosamalitsa,” anatero Mkwinda.

Source Link

Let us know what you think of this article and remember to add us on our facebook and follow us on our twitter. Come back daily for more Malawi business news.

Quick Links: Download Business eBooks | Ten Signs You Are An Entrepreneur | What is a Managing Director?

The post Owina Lotto agula nyumba ndi galimoto – appeared first on Business Malawi.

マラウイニュースメルマガ登録

メルマガ限定配信のマラウイ超ローカルニュースが無料で受け取れます

マラウイ・アフリカ・国際協力に興味があったら登録しよう!

プライバシーポリシーについてはこちらを確認してください

コメントを残す

メールアドレスが公開されることはありません。 が付いている欄は必須項目です