Bwato Satsitsilana Pakati Pa Nyanja- Micheal Usi Wauza MCP

Nduna Yowona zokopa Alendo, a Micheal Usi, omwenso ndi wachiwiri kwa President wa chipani cha UTM, wauza President Lazarus Chakwera kuti chipani cha UTM chilibe lingaliro lotuluka mu Mgwirizano wa Tonse.

A Usi ayakhula izi Loweruka pa mwambo okumbukira mtsogoleri wakale wa dziko lino, a Dr. Hastings Kamuzu Banda, omwe ukuchitikira mu mzinda wa Lilongwe.

Mawu a Usi abwera pomwe akulu-akulu ena a chipani cha Malawi Congress (MCP) akufuna kuti chipani cha UTM chituluke mu Mgwirizano wa Tonse.

Usi ati kukakamiza UTM kutuluka mu Mgwirizano wa Tonse m’chimodzimodzi kukakamiza munthu kuti atsike mu bwato lili pakati pa Nyanja, zomwe malingana ndi a Usi ndi ichi ndi chipongwe komanso mwano.

Bwato satsitsilana pakati pa Nyanja,” anatero a Usi, powonjezera kunena kuti chipani cha UTM chipitiliza kulemekeza Mgwirizano wa Tonse.

Ndunayi yauzanso President Dr. Chakwera kuti achotse ntchito kagulu kena ka anthu komwe kakufuna kusokoneza Boma Lake.

The post Bwato Satsitsilana Pakati Pa Nyanja- Micheal Usi Wauza MCP appeared first on Malawi Voice.

マラウイニュースメルマガ登録

メルマガ限定配信のマラウイ超ローカルニュースが無料で受け取れます

マラウイ・アフリカ・国際協力に興味があったら登録しよう!

プライバシーポリシーについてはこちらを確認してください

コメントを残す

メールアドレスが公開されることはありません。 が付いている欄は必須項目です