TIYENI TONSE TIKAPEREKE: Akhiristu a CCAP awalamula kupereka K10,000 aliyense  

Katswiri amene anapeka nyimbo ya ‘Ayambe Ku mbuyo ko, Ayambe ku mbuyo ko tikapereke eee, tiyeni tonse tikapereke’ m’kulinga anali ataziwona.

Lero mpingo wa CCAP mu Synod ya Blantyre yapempha akhiristu ake kupereka ndalama yokwana K10, 000 aliyense yothandizira kubweza ngongole yokwana K2 billion yomwe mpingo wu uli nayo.

Kalata yomwe yawelengedwa lero mipingo yonse yomwe yili pansi pa synod-yi, yalamulanso abusa onse kupereka ku Synod 10 kwacha pa 100 kwacha ili yonse ya chakhumi chomwe azitolera sabata ndi sabata.  

Malingana Mlembi wamkulu mu Synod ya Blantyre, Reverend Anderson Juma, zina mwa ngongolezi akuti ndi misonkho komanso zina zomwe Synod yi idatenga ku ma bank osiyasiyana m’dziko muno.

M’busa Juma anawonjezera kunena kuti ndalama zimene akhiristu a mpingo wu amapereka kudzera mu zopereka za malonjezano sizikukwanira poyendetsa ntchito za mpingo.

Ichi, ati n’chifukwa chake Synod ya Blantyre yakhala ikupempha akhiristu kuti azipereka molowa manja.

The post TIYENI TONSE TIKAPEREKE: Akhiristu a CCAP awalamula kupereka K10,000 aliyense   appeared first on Malawi Voice.

マラウイニュースメルマガ登録

メルマガ限定配信のマラウイ超ローカルニュースが無料で受け取れます

マラウイ・アフリカ・国際協力に興味があったら登録しよう!

プライバシーポリシーについてはこちらを確認してください