Mutharika Alonjeza Kukonzanso Malawi

Mtsogoleri wa chipani cha Democratic Progressive (DPP), Peter Mutharika walonjedza kukonza dziko lino lomwe akuti lawonongedwa ndi ulamuliro wa Lazarus Chakwera.

A Mutharika, omwenso akuzapikisana nawo pa chisankho cha mchaka cha mawa, anena izi kudzera pa tsamba lawo la mchezo lapa facebook.

Pamenepa, iwo apempha a Malawi kuti agwirane manja maka pokozanso dziko lowonongekali.

Mawu a Mutharika abwera pomwe kwangosala masiku ochepa kuti achititse msonkhano wa ndale mu mzinda wa Blantyre.

Mwa zina, iwo akuyembekezereka kufotokozera a Malawi mfundo zomwe akonza pokozanso dziko la Malawi.

The post Mutharika Alonjeza Kukonzanso Malawi appeared first on Malawi Voice.

マラウイニュースメルマガ登録

メルマガ限定配信のマラウイ超ローカルニュースが無料で受け取れます

マラウイ・アフリカ・国際協力に興味があったら登録しよう!

プライバシーポリシーについてはこちらを確認してください