Aphungu akukambirana za chamba

Aphungu a nyumba ya malamulo akukambirana ganizo lokhazikitsa lamulo lomwe lingavomereze ulimi wa chamba chosuta m’dziko muno.

Phungu wadera la kum’mwera kwa boma la Lilongwe, a Peter Dimba, ndiyemwe wabweretsa ganizolo mnyumbayi.

Ena mwa maganizo omwe aphungu apereka pothilira ndemanga ndikuti lamulo lovomereza ulimiwu lidzakhale lokomera alimi achimalawi kuti ambiri adzakhale ndi mwayi opeza phindu lochuluka komanso kupereka mwayi wa ntchito.

Aphunguwa ati, mwazina, ulimi wa chamba utha kuthandiza dziko lino kupeza ndalama zakunja zochuluka.

Ndipo Mtsogoleri wa zokambirana mu nyumbayi, a Richard Chimwendo Banda, ati ulimiwu ndi wabwino koma ndikofunika kuti amalawi aphunzitsidwe zokhudza ulimiwu poopa kubweretsa mavuto pakati pa achinyamata.

Padakali pano, aphunguwa akupitiriza kupereka maganizo awo pa nkhaniyi.-( Credit: MBC Online)

The post Aphungu akukambirana za chamba appeared first on Malawi Voice.

マラウイニュースメルマガ登録

メルマガ限定配信のマラウイ超ローカルニュースが無料で受け取れます

マラウイ・アフリカ・国際協力に興味があったら登録しよう!

プライバシーポリシーについてはこちらを確認してください