Aphungu a MCP avomereza ulimi wa Chamba

Aphungu a chipani cha Malawi Congress (MCP) avomereza lamulo lolola ulimi wa chamba m’dziko muno.

Aphungu wa avomera lamuloli mnyumba ya malamulo m’mawa la Lachinayi ponena kuti ulimi wa chamba utha kukweza chuma cha dziko lino.

Panthawi yomwe amavomeleza biluyi aphungu ena achipani cha DPP anatuluka mnyumbayi ponena kuti lamuloli ndilosayenera.

Malingana ndi aphungu wa, yemwe anabweresa bill yu a Peter Dimba sanafikire nthambi zingapo zokhudzidwa.

Koma, mtsogoleri wa zokambirana mnyumbayi a Richard Chimwendo Banda, wati cholinga cha biluyi sikuvomeleza kuti anthu adzisuta chamba koma kulima chambachi.

Ulimi wa chamba, malingana ndi a Dimba, utha kubweretsa ndalama zakunja mdziko muno zokwana pafupifupi 700 Million Dollars pa Chaka.

The post Aphungu a MCP avomereza ulimi wa Chamba appeared first on Malawi Voice.

マラウイニュースメルマガ登録

メルマガ限定配信のマラウイ超ローカルニュースが無料で受け取れます

マラウイ・アフリカ・国際協力に興味があったら登録しよう!

プライバシーポリシーについてはこちらを確認してください