Anthu ena akufuna kundiyambanitsa ndi a Chilima, atero a Chakwera

Mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera ati pali kagulu kena ka anthu komwe kakufuna ku wayambanitsa iwo ndi wachiwiri wawo a Saulos Chilima.   

A Chakwera anena izi lero pa msokhano wa chitukuko pa bwalo la za masewera la Chinsapo mu mzinda wa Lilongwe.

M’mawu awo anati anthu ena amakonda kudanitsa komanso kuyambanitsa anthu ndipo ayesera kangapo konse kudanitsa iwo ndi a Chilima koma alephera.

“Ndikuziwa kuti pali anthu ena omwe akufuna kutiyambinitsa ndi a Chilima komanso zina mwa nduna zanga,” anatero a Chakwera

Malingana ndi a Chakwera, iwo sapanga nawo ndale zodanitsa, zotukwana ena komanso zonyoza ena.

Pamenepa a Chakwera anapempha a Malawi komanso a ndale ena kuti asiye ndale zosungirana ka m’peni ku mphasa.  

Iwo ati a nthawi yakwana kuti a Malawi agwirane manja pa ntchito yotukula dziko lino osati kungokhalira ‘ukavundula madzi’.  

Pakhala pali phekesera zoti a Chakwera omwe ndi a chipani cha Malawi Congress (MCP) komanso a chiwiri awo a Chilima a chipani cha UTM akhala asakugwirizana.

The post Anthu ena akufuna kundiyambanitsa ndi a Chilima, atero a Chakwera appeared first on Malawi Voice.

マラウイニュースメルマガ登録

メルマガ限定配信のマラウイ超ローカルニュースが無料で受け取れます

マラウイ・アフリカ・国際協力に興味があったら登録しよう!

プライバシーポリシーについてはこちらを確認してください